chchichewa survivors-se 20200608

27
Opulumuka Kusindikiza kwa Padera CHICHEWA: SURVIVORS-SE

Upload: others

Post on 11-Apr-2022

1 views

Category:

Documents


0 download

TRANSCRIPT

Page 1: chChichewa Survivors-SE 20200608

OpulumukaKusindikiza kwa PaderaCHICHEWA: SURVIVORS-SE

Page 2: chChichewa Survivors-SE 20200608

1

Malonje kwa Wopulumuka!

Buku lino ndi lanu. Lili ndi fundo zambiri ndiponso

zinthu zoti muchite zambiri. Likuthandizani kuchira ndi kukula.

Mliri wa COVID-19 wakhudza munthu aliyense m’njira zosiyanasiyana.

Choncho buku lanuli ndi losiyana ndi mabuku a anthu ena onse.

Limeneli ndi lanulanu!

Dzina langa ndi

Ine ndine Wopulumuka

Page 3: chChichewa Survivors-SE 20200608

2 3

Kukhala ModzitetezaMwina mukumadandaula kapena

kuchita mantha.Sikuti mukulakwitsa kutero ayi.

Munthu wopulumuka pa ngozi nthawi zina amachitanso mantha.M’dziko lonse lapansi muli zinthu

zambiri zodabwitsa. Komanso muli zina zochititsa mantha kwambiri. Monga

kusefukira kwa madzi, nkhondo, ngozi za galimoto ndipo tsopano kwabwera mliri pa dziko lonse (matenda amene akufalikira ponseponse mofulumira kwambiri amene asanduka mliri).

Lembani zinthu zingapo zomwe zikukudandaulitsani za mliri wa COVID-19:

Page 4: chChichewa Survivors-SE 20200608

4 5

Ndinati, “Ndithu, ndikanakhala ndi mapiko ankhunda!Ndikanawulukira kutali ndi kukapuma.

Ndikanathawira kutalindi kukakhala m’chipululu.

Ndikanathamangira kumalo anga a chitetezo;kutali ndi mphepo yaukali ndi yamkuntho.”

Pali munthu wina amene ankachita mantha kwambiri pamene

ankalemba zomwe ankazifuna.

Salimo 55:6–8

Page 5: chChichewa Survivors-SE 20200608

6 7

Kodi inu munakhalapo ndi maganizo monga amenewa?

Kodi pamene mukuchita mantha mumafuna chitakuchitikirani chiyani?

Pamene ndili ndi mantha, ndimalakalaka…

Lembani kapena jambulani chomwe mukufuna apa.

Alemekezeke Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu, Atate achifundo chonse, Mulungu

wachitonthozo chonse. Iye amatitonthoza ife m’mavuto athu onse,

kuti ifenso tithe kutonthoza amene ali pavuto lililonse

ndi chitonthozo chimene ife tilandira kwa Mulungu.

2 Akorinto 1:3–4

Have you ever made a wish like this? What do you wish when you are afraid?

Give praise to the God and Father of our Lord Jesus Christ!

He is the Father who gives tender love. All comfort comes from him.

He comforts us in all our troubles. Now we can comfort

others when they are in trouble.We ourselves receive comfort from God.

2 Corinthians 1:3–5Write or draw your wish here.

Page 6: chChichewa Survivors-SE 20200608

8 9

Malangizo kwa Opulumuka

Pempherani: Nthawi zonse pamene mukuchita mantha muziyankhula ndi Mulungu. Iye adzakhala malo anu achitetezo.

Chitanipo Kanthu!

Pekani nyimbo.Nyimbo ndi zabwino kwambiri

pakuti zimathandiza anthu kuchotsa mantha.

Nayi nyimbo yochokera m’Baibulo

Yehova ndiye kuwunika kwanga ndi chipulumutso changa;

ndidzaopa yani?Yehova ndi linga la moyo wanga;

ndidzachita mantha ndi yani?

Salimo 27:1

Sambani m’manja ndi sopo pafupipafupi.

Imani motalikirana ndi anthu ena.

Onetsetsani kuti simukukhudza maso anu, mphuno yanu ndi pakamwa panu.

Ngati thupi lanu likupweteka, ngati mukutsokomola kapena mukubanika popuma, wuzani makolo anu kapena amene akukuyang’anirani kuti awuze dotolo.

Muzichita masewero m’nyumba ndi a pa banja panu m’malo mokaswera ndi anzanu kunja.

Dzitetezeni ku kachirombo ka corona:

Page 7: chChichewa Survivors-SE 20200608

10 11

Kupempha Thandizo

N’kutheka kuti mwathedwa nzeru.Sikuti mukulakwitsa kutero.

Opulumuka amafunanso thandizo nthawi zina.

Zimakhala zopweteka kwambiri pamene munthu ukulephera kutuluka m’nyumba kapena kusowa wosewera naye. Mumakhala wosangalala kapena

wokwiya. Zimavuta kuti mufotokoze bwino momwe mukumvera mu mtima mwanu.

Zimakhala zovuta kulandira thandizo kuchokera kwa anthu ena.

Anthu ambiri akufuna kukuthandizani. Koma sangathe kutero chifukwa sakudziwa

zomwe mukuzisowa, choncho…AWUZENI!

Page 8: chChichewa Survivors-SE 20200608

12 13

“Chifukwa chake pempherani motere:“ ‘Atate athu akumwamba, dzina lanu lilemekezedwe,

Ufumu wanu ubwere, chifuniro chanu chichitike

pansi pano monga kumwamba.Mutipatse chakudya chathu chalero.

Mutikhululukire mangawa athu, monga ifenso tawakhululukira

amangawa athu.Ndipo musatitengere kokatiyesa;

koma mutipulumutse kwa woyipayo.”

Mateyu 6:9–13

Iye anati,

Pemphani kwa Mulungu chomwe mukufuna!

Yesu anatiphunzitsa momwe tingapemphere thandizo kwa Mulungu.

Page 9: chChichewa Survivors-SE 20200608

14 15

Tili ndi mwayi wopempha thandizo nthawi zonse kwa Mulungu.

Tengani pemphero lomwe lili pa peji yotsatirayi kukhala pemphero lanu

ndipo onjezerani mawu anu.

Yehova ndiye mphamvu zanga ndi chishango changa;mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa.

Mtima wanga umalumphalumpha

chifukwa cha chimwemwendipo ndidzayamika

Iye m’nyimbo.

Salimo 28:7

Mulungu Atate wokondedwa,ndikuthokoza chifukwa

mumandikonda ine kwambiri.Lero ndikumva mu mtima mwanga

chifukwa cha

ndipo ndikufuna thandizo lanu. Chonde

Zikomo chifukwa

Page 10: chChichewa Survivors-SE 20200608

16 17

Malangizo kwa Opulumuka

Fotokozerani anthu zomwe mukusowa pa moyo wanu.Afotokozereni anthu momwe angakuthandizireni.

Pemphero lodzipempherera nokha.Pemphani Mulungu kuti akusungeni ndi kuteteza banja lanu.Thokozani Mulungu chifukwa chokusamalirani.

Khalani wothandiza wina. Yang’anani munthu amene akusowa thandizo.

Mutha kuthandiza amene ali pafupi ndi nyumba yanu,

posamalira m’nyumba mwawo, kapena kutsuka mbale zawo.

Munthu umamva bwino ukamathandiza ena!Kumbukirani kupempha thandizo pamene mukufuna kuthandizidwa.

Chitanipo Kanthu!

Page 11: chChichewa Survivors-SE 20200608

18 19

Salimo 10:14

Kufuna Chitonthozo

Mwina muli ndi chisoni.Sikuti mukulakwitsa kutero.Opulumuka amamvanso chisoni nthawi zina.

Mwina mukumusowa mnzanu amene anamwalira.

Mwina mukuganiza kwambiri za mmene zinthu zinalili kale. Mwina simukutha kumvetsa

zomwe zikukuchitikirani.

Komatu Inu Mulungu, mumazindikira mavuto ndi zosautsa,

mumaganizira zochitapo kanthu.

Page 12: chChichewa Survivors-SE 20200608

20 21

Odala ndi amene ali achisoni,chifukwa adzatonthozedwa.Odala ndi amene ali ofatsa,

chifukwa adzalandira dziko lapansi.Odala ndi amene akumva njala

ndi ludzu la chilungamo,chifukwa adzakhutitsidwa.

Odala ndi amene ali ndi chifundo,chifukwa adzawachitira chifundo.Odala ndi amene ali oyera mtima,

chifukwa adzaona Mulungu.Ndi odala amene amabweretsa mtendere,

chifukwa adzatchedwa ana a Mulungu.Odala ndi amene akuzunzidwa

chifukwa cha chilungamo,pakuti ufumu wakumwamba ndi wawo.”

Mateyu 5:4–10

Ambuye Yesu anati,

Page 13: chChichewa Survivors-SE 20200608

22 23

Kodi ndi ziti zomwe mumakonda kuchita?

Kodi mumakonda kuthamanga mwaliwiro? Kodi mumakonda kusaka tizirombo tooneka modabwitsa?

Kodi mumakonda kujambula?

Lembani mndandanda wa Zinthu Zofunika Kuchita. Lembani zomwe mumakonda kuchita.

Zinthu Zofunika Kuchita

Page 14: chChichewa Survivors-SE 20200608

24 25

Malangizo kwa Opulumuka

Uzani munthu amene mumamukonda zomwe inu mukumva mu mtima mwanu. Zimathandiza kufotokozera wina maganizo anu ndi zomwe mukumva mu mtima mwanu.

Muuzeni Mulungu za chisoni chanu. Mupempheni kuti akutonthozeni. Yembekezerani dalitso.

Chitanipo kanthu pa Zinthu Zofunika Kuchita zija.

Chitanipo Kanthu!

Pangani Bokosi la Zochitika.

Pezani bokosi.

Kongoletsani bokosilo ndi penti kapena chekenirani ndi chilichonse chokongoletsa.

M’bokosimo muyikemo zinthu zosangalatsa. Zinthu za fungo labwino lomwe mumalikonda, zinthu zokoma, zomveka bwino.

Pamene muli ndi chisoni, tengani Bokosi la Zochitika ndipo muyambe kuseweretsa zinthu zomwe zimakusangalatsanizo.

Page 15: chChichewa Survivors-SE 20200608

26 27

Zisiyeni Zipite

Mwina mwakwiya.Sikuti mukulakwitsa kutero.Nthawi zina Opulumuka amakwiyanso.

Mwina mukuona kuti zinthu sizikuyenera kutero.Mwina mwakwiya chifukwa simukuloledwa kutuluka m’nyumba. Mwina mukanakonda zinthu zikanachitika mwa mtundu wina.

Jambulani nkhope ya munthu wokwiya apa, ngati inu mwakwiya.

GRRRRR!

Page 16: chChichewa Survivors-SE 20200608

28 29

N’zosalakwika kukwiya,koma ndi zabwino kwambiri kuchotsa mkwiyo.

Nthawi zonse tikuyenera kukhululukira munthu wina pa zomwe watichitira zimene

zikutipweteka mu mtima. Choncho tikuyenera kuchotsa mkwiyo wathu.

ndi kuchotsa mkwiyo.Ndinu anthu osankhidwa ndi Mulungu, oyera mtima ndi okondedwa kwambiri,

muvale chifundo, kukoma mtima, kudzichepetsa, kufatsa ndi kupirira.

Mulezerane mtima ndipo muzikhululukirana ngati wina ali ndi chifukwa ndi mnzake.

Muzikhululukirana monga Ambuye anakhululukira inu.

Akolose 3:12–13

Kukhala moyo umene Mulungu amafuna

zikutanthauza kukhala ndi mphamvu zokhululukira anthu.

Page 17: chChichewa Survivors-SE 20200608

30 31

Nthawi zina pamafunika kufuula kwambiri kuti muchotse mkwiyo wanu.

Pangani Chinthu Chofuulira.

2. Gunditsani pakamwa panu mbali imodziyi.3. Dzanja lanu ligwire mbali ina ya chinthuchi. 4. Mukokere mpweya m’kati.5. Fuulani kwambiri monga momwe mungathere.

1. Pindani bukuli motere.

Page 18: chChichewa Survivors-SE 20200608

32 33

Malangizo kwa OpulumukaKhululukirani anthu. Pemphani Mulungu kuti akupatseni mphamvu zokhululukira anthu amene anakulakwirani.

Chotsani mkwiyo. Gwiritsani ntchito Chinthu chanu Chofuulira chija.

Chitanipo kanthu!Njira yosavuta yopewera mkwiyo.

Muganize inuyo kuti ndinu munthu winayo. Kodi zikusintha ndi ziti pa moyo wanu pamene mukuona zinthu monga mmene akuonera winayo?

Mukokere mpweya m’kati musanayankhe.

Gonani mokwanira.

Kwiyani koma musachimwe. Dzuwa lisalowe mukanali

chikwiyire.Aefeso 4:26

Pitani kakhululukireni!

Page 19: chChichewa Survivors-SE 20200608

34 35

Kulumikizana ndi Ena

Mwina mukudziona kuti muli nokha.Sikuti mukulakwitsa kutero.Opulumuka nthawi zina amadziona ngati ali okha.

Mwina mukuona kuti dzikoli lakukulirani ndipo inu mukudziona kuchepa kwambiri.

Mwina mukumusowa mnzanu amene mumamukonda.Mwina muli kutali ndi abwenzi anu kapena banja lanu.

Ngati mwamusowa wina wake, lembani dzina la munthuyo pano.

Mulikongoletse dzinalo kuti lioneka ngati munthuyo ali pamenepo.

Pangani kuti dzinalo likongole kwambiri kapena lioneka ngati chidole,

kapena LIKULE KWAMBIRI kapena lichepe kwambiri.

Page 20: chChichewa Survivors-SE 20200608

36 37

Iye ndi Atate wa ana amasiye, mtetezi wa amayi amasiye,

ndiye Mulungu amene amakhala m’malo oyera.

Mulungu amakhazikitsa mtima pansi osungulumwa m’mabanja.

Kuyambira pachiyambi cha dziko, Mulungu anati sikwabwino kuti ife tikhale tokha.

Khalani bwenzi!

Salimo 68:5–6

Zimatengera gulu lonse kuti munthu akhale moyo wabwino.

Page 21: chChichewa Survivors-SE 20200608

38 39

Ngati mukuona kuti muli nokha, yambani kucheza ndi anthu amene akuyandikirani.

Zolemba zanu zikhale zosangalatsa kwambiri!

Njira ina yabwino kwambiri yoyambira kucheza ndi anthu ndi kuwalembera kalata.

Mawu amene mulembewo adzakhala njira yolumikizirana ndi munthu wina.

Mutha kulemba mawu Owathokoza,

mawu a Chilimbikitso,

mawu akuti, Ndakusowani kapena mawu akuti,

Kodi sukufuna kukhala ndi kachidole kokhala ngati nyama ya kuthengo?

Page 22: chChichewa Survivors-SE 20200608

40 41

Malangizo kwa OpulumukaYang’anani mbali zonse ndipo yamikani Mulungu chifukwa cha anthu abwino amene mukukhala nawo.

Pezani ndi kulumikizana ndi munthu wina polemberana naye.

Chitanipo kanthu!

Phunzirani kukonda anthu amene mukukhala nawo ndi chikondi monga ichi:

Chikondi n’choleza mtima, chikondi n’chokoma mtima, chilibe nsanje, sichidzikuza, sichidzitamandira. Chikondi chilibe mwano, sichodzikonda, sichipsa mtima msanga,

sichisunga mangawa. Chikondi sichikondwera ndi zoyipa koma chimakondwera ndi choonadi. Chimatchinjiriza

nthawi zonse, chimakhulupirika nthawi zonse, chimakhala ndi chiyembekezo nthawi zonse, chimapirira

nthawi zonse. Chikondi n’chosatha. Koma mphatso ya uneneri idzatha, pamene pali kuyankhula malilime

adzatha, pamene pali chidziwitso chidzatha.1 Korinto 13:4–8

Page 23: chChichewa Survivors-SE 20200608

42 43

Pamene Zonse Zatha Mulungu ndiye kothawira kwathu ndi mphamvu yathu,

thandizo lopezekeratu pa nthawi ya mavuto.

N’chifukwa chake sitidzaopa ngakhale dziko lapansi lisunthike,

ngakhale mapiri agwe pakati pa nyanja,

ngakhale madzi ake atakokoma ndi kuchita thovu,

ngakhale mapiri agwedezeke ndi kukokoma kwake.

Salimo 46:1–3

Inu simukudzwa kuti mliri umenewu ukhalapo mpaka liti.Koma mungathe kudalira Mulungu kuti akudutsitsani.Koma nthawi ino, mutha kuyamba kukonzekera zomwe

mukufuna kudzachita pamene izi zonse zatha!Lembani zinthu zomwe mukufuna kudzachita

Page 24: chChichewa Survivors-SE 20200608

44 45

Baibulo likutiwuza kuti:

Pakuti Mulungu anakonda dziko lapansi, kotero anapereka Mwana wake wobadwa yekha, kuti aliyense wokhulupirira Iye asatayike koma

athe kukhala ndi moyo wosatha.

Yohane 3:16.

Yesu anafa pa mtanda chifukwa cha machimo athu, koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa patatha

masiku atatu ndipo ali ndi moyo mpaka lero!

Yesaya 53:4

Yesu akufuna kuti inu mumudalire ndi kupereka moyo wanu kwa Iye kuti Iyeyo azikhala ndi inu nthawi zonse. Ngati ndinu wokonzeka kupereka moyo wanu

kwa Yesu, pempherani pemphero ili.

Ambuye Yesu,

ine ndikudziwa kuti mumandikonda ndipo munandifera pa mtanda.

Ndikupepesa chifukwa cha zinthu zoyipa zimene ndakhala ndikuchita, ndipo kuyambira lero ndikufuna kukhala moyo wokondweretsa Inu.

Lamulirani moyo wanga pamene ndikuphunzira kutsatira Inu.

Zikomo chifukwa chokhala Mpulumutsi wanga!

Ameni.

Iye anamva zowawa m’malo mwa ife;ndipo anasautsidwa m’malo mwathu.

Page 25: chChichewa Survivors-SE 20200608

46 47

Page 26: chChichewa Survivors-SE 20200608

48

Page 27: chChichewa Survivors-SE 20200608

OpulumukaTM Kusindikiza kwa PaderaMwini © 2020 ndi Biblica, Inc.

Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.

The SurvivorsTM Special Edition (Chichewa)Copyright © 2020 by Biblica, Inc.

All rights reserved worldwide.

Mawu a Mulungu achokera mu m'Baibulo laMawu a Mulungu Mu Chichewa ChaleroTM

Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.

Zizindikiro izi “Biblica”, Biblica Logo, “International Bible Society” ndi zovomerezeka ku Amerika ndi Bungwe la Biblica.

ISBN: 978-1-62337-395-5